Chichewa Christian Hymns
Hymn 247 MULUNGU anditsogolera,
MULUNGU anditsogolera,
Ndapumula m’mtimamo;
Ayang’anira njira zanga
Nsiku zanga zonsezo.
Mulungu anditsogolera
Nsiku zanga zonsezo;
Ndidzatsatira Mbuye wanga
M’njira mwake momwemo.
Masiku ena pali mdima,
Ndivutidwa m’mtimamo;
Masiku ena ndikondwera
Ndi zabwino zangazo.
Masiku onse m’mtima mwanga
Ndili ndi mtenderewo,
Chifukwa ndimakhulupira
Mtsogoleri wangayo.