Chichewa Christian Hymns
Hymn 297 POKUMANA m’mayesero a dziko lino,
POKUMANA m’mayesero a dziko lino,
Matenda, imfa ndi usiwa;
Moyo umalefuka,
Ndikugwetsedwa mphwayi;
Mpaka nditamuuza Yesuyo.
Um fotokozere Yesu vuto lako,
Um fotokozere Yesu zonsezo;
Um’fotokozere Yesu vuto lako;
Adzakuchitira chifundo.
Pokumana m’mayesero a dziko lino,
Ndinasokera kutaliko;
Yesu nandigwira dzanja,
Nanditsogolera;
Mmene ndinamuuza zonsezo.
Abale tisachedwe ndi za dziko lino,
Za dziko lino ndi zachabe;
Yesu akufuna tibwere kwa Iye lero,
Kuti timuuzetu zonsezo.