Chichewa Christian Hymns
Hymn 150 MIPINGO iyo idzatu,
MIPINGO iyo idzatu,
Yoyenda mangu pajapo,
Afuma kuti anthuwo?
Afika bwanji komweko?
Anena anthu onsewo,
“Yesu Sing’anga apitapo.”
Anena anthu onsewo,
“Yesu Sing’anga apitapo”
Azizwa anthu ajawo,
Nafunsa, “Ndani mlendoyo?
Wanzeru monga Iyeyo
Kulibe wina konseko.”
Ndi Yesu yemwe kalelo,
’Nakhala munthu pansipa;
Anthenda onsenthaŵiyo
Nachirayake mphamvuyo
Afika Yesu leroli,
Chifundo m’mtima wakemo,
Timfitse msanga kwathuko
Akhale nafe ponsepo.
Timsankhe Yesu Mbuyeyo,
Timyese Mfumu yathuyo,
Chifukwa tikamkanatu
Tikhala otayikawo.
Tsopano inu’dzanitu,
Asanapitirirepo.
Tsopano inu’dzanitu,
Asanapitirirepo