Chichewa Christian Hymns
Hymn 30 YEHOVA, Mbusa wangadi,
YEHOVA, Mbusa wangadi,
Ndilibe kusoŵa;
Andigonetsa bwinoli
Mumsipu wokoma.
Ku madzi ake odikha
Anditsogolera;
Ndi moyo wanga wofoka
Aulimbikitsa.
Anditsogolera m’njira
Zakulungamazo;
Chifukwa changa ay’, koma
Cha dzina lakelo.
Ndipyola kodi chikhwaŵa
Cha mthunzi wa imfa?
Ndilibe mantha ngati ’Nu
Mundiperekeza.
Chakudya changa chabwino
Mwandikonzera pha!
Pamaso pa adaniwo
Mudyetsa mtimanga.
Mwadzoza mutu wanga ndi
Mafuta okoma;
Mwadzadza chikho changadi,
Inde, chisefuka.
Zokoma ndi zakuyanja
Zidzanditsatako;
Ndikhala m’nyumba ya Mlungu
Ku nthaŵi zonsezo.