Chichewa Christian Hymns
Hymn 57 TIYENI, dzalireni nane,
TIYENI, dzalireni nane,
Tidze ku mtanda wa Ambuye,
Tionse tichitetu maliro;
Wapachikidwa Ambuyathu.
Kodi misozi itisoŵa,
Poona anthu amanyoza?
Onani umo apirira;
Wapachikidwa Ambuyathu.
Anena mawu m’mtanda momwe
Mawu ochepa achifundo,
Apempherera ’dani ake;
Wapachikidwa Ambuyathu.
Mtima wangawe, uyenera
Kuduka ndi manyazi lero,
Zamlasa ndi zoipa zako;
Wapachikidwa Ambuyathu.
Ona chikondi cha Mulungu,
Ona zoipazo za anthu,
Koma chakula ndi chikondi;
Wapachikidwa Ambuyathu.