Chichewa Christian Hymns
Hymn 51 PANTHAWI yakufa Ambuye,
PANTHAWI yakufa Ambuye,
Anthu ananena:
“Dzipulumutsetu pamtandapo.”
(M) Yesu ndi mawu aakulu,
(O) Anafuula;
(M) Yesu ndi mawu aakulu,
(O)Anafuula;
“Eloyi, Eloyi
Mulungu wanga,
Mwandisiiranji,
Mwandisiiranji?”
Imfa ya Bwenzi lathu Yesu,
Yomvetsa chisoni;
Ophunzira onse anathaŵa.
Pamene anakhomedwatu,
Pamtanda Yesuyo;
Zoipa zathu zinam’psinja ‘Ye.
Imfa yake ndi yopambana,
Yotipulumutsa;
Yotitengera ife mtendere.