Chichewa Christian Hymns
Hymn 481 USACHIMWE konse,
USACHIMWE konse,
Lekatu kukwiya;
Uli mwana wake,
Mwana wa Mbuyathu.
Yesu ndi wofatsa,
Yesu ndi woyera;
Ana ake omwe
Aziyera m’mtima
Mzimu wakuipa
Ukusuzumira,
Umakuyesera
Kuti ukachimwe.
Koma usalole
Mawu a Satana;
Bweza tchimo lake,
Chita zolungama.
Yesu ndi Mbuyako,
Mbuyeyo ngwabwino;
Ana ake omwe
Aziyera m’mtima.