Chichewa Christian Hymns
Hymn 41 MKATI mwa zovuta zathu
MKATI mwa zovuta zathu
Yesu aitana ife,
Tsiku lonse amanena:
“Tsata Ine mkristu iwe.”
Kale ophunzira ake
Namvanso kunyanja kwawo,
Zinthu zonse anasiya
Kukatsata Mbuye wawo.
Yesu atiuze ife;
Tikakonda chuma chokha,
Ati Yesu; “Mwana wanga,
Undikondetu koposa.”
Mwachimwemwe, mwachisoni,
Pogwiritsa ntchito zonse,
Aitana Mpulumutsi
Kuti tizimkonda tonse.
Yesu ayitana ife;
Mbuye, mutimvetse ndithu,
Tipereke mtima wathu,
Tikondane lero ndithu.