Chichewa Christian Hymns
Hymn 24 TITAME Mlungu Wakumwamba,
TITAME Mlungu Wakumwamba,
Timwimbire nyimbo,
Kukoma kwake kwatipatsa
Zonse tili nazo.
(Timwimbire nyimbo,
Timwimbire nyimbo!
Kukoma kwake kwatipatsa
Zonse tili nazo)
Poyamba paja analenga
Zonse dziko muno,
Tsopano lomwe azisunga
Zonse zili moyo.
Tinasokera ngati nkhosa,
Moyo tinataya,
Tinakondwera ndi zoipa
Zonse tinatsata.
Komweko titasaukira,
Titafuna kufa,
Atate anatilondola
Naitana ife.
Tiyeni tizipita kwathu,
Tisasokerenso,
Tilape m’mtima kuti
tikakhale ndi Mulungu.