Chichewa Christian Hymns
Hymn 372 DZUŴA la Mulungu
DZUŴA la Mulungu
Ladzatu labwino;
Ndi chimwemwe ife
Tiliona lero.
Lithaŵitsa nkhaŵa,
Lichotsanso mantha
Ndimo m’mtima mwathu
Likhalitsa bata.
Tikondwera kuti
Tipumula lero;
Tazileka ntchito
Kuti tipemphere.
Koma ntchito zathu
Za palero lino
Nzakumvera Yesu,
Kumlandira bwino.