Chichewa Christian Hymns
Hymn 356 YESU Mbuye onani,
YESU Mbuye onani,
Tadza poyitana Inu;
M’dzina lanu tifika,
Osekera kwa Atate.
M’khale nafe Inu nokha,
Tikayimba n’kupemphera.
Mbuye, Mzimu Woyera,
Munapatsa ana anu;
Kukalonga mumtima,
Mawu ndipo mvano womwe.
Zinthu zonse pansi pano,
Sizikondweretsa ife.
Mzimu, m’longe m’mtimamo,
Maphunziro achifundo;
Timve lero ndi mawa,
Ndi masiku onse: Yesu!
Ndipo M’mwamba tidzawona,
Tidazimva pansi pano.