Chichewa Christian Hymns
Hymn 354 ATATE, tifika pamaso panu;
ATATE, tifika pamaso panu;
Mukomane ndi ife, Mbuye wathu.
Mitima yathu iyi nayo njanu,
Muiyeretse, muikonze Mbuye.
Ndi maso athu awa nawo nganu,
Muŵapenyetse zinthu zanu zokha.
Ndi manja athu awa nawo nganu,
Agwiretu ntchito yanu yokhayo.
Ndi miyendo yathu iyinso njanu,
Ithamange m’ntchito yanu yokhayo.
Ndi milomo yathu iyinso njanu,
Ilalike Mawu anu kwa onse.
Ndi makutu athu awanso nganu,
Muŵamvetse Mawu anu okhawo.
Tidziperekadi konse kwa Inu
Tikakhale anthu anu okhawo.