Chichewa Christian Hymns
Hymn 282 INU muli mehere,
INU muli mehere,
Wa dziko lapansi;
Ukasukuluka,
Sungakolerenso,
Yang’anani bwino,
Muyende m’njirayo;
Kuti mungagwetu,
M’zovuta za dziko.
Pamenepo sungakwanirenso kanthu,
Koma kuti ukaponyedwetu kunja.
Ndinu kuunika,
Kwa dziko lapansi;
Mudzi wapaphiri
Sungabisiketu.
Sungayatse nyali,
N’kuyivundikira;
Koma uyika pachoikapo chake.
Ndipo iwunikira onse
m’nyumbamo;
Chomwecho inu
muunikire dziko.
Kuti pakuwona,
Ntchitozo zabwino;
Alemekezedwe,
Mlungu ‘Tate wanu.