Chichewa Christian Hymns
Hymn 256 NGATI mtima sumakonda
NGATI mtima sumakonda
Yesu supumula bwino;
Mbuye, suwu mtima wanga,
Ndiwo wanu, mulandire.
Dziko lonse ndilitaya;
Ndikondetsa Yesu Mbuye;
An’komera kopambana
Andikondweretsa ndiye.
Ndakudani, mnandikonda
Ndi kukhetsa mwazi wanu.
Simuleka kundikonda;
Ine sindidzalekanso.
Mndisungire mtima wanga,
Uzikhulupira Inu,
Kuti moyo wanga wonse
Ubisaletu mwa Yesu.