Chichewa Christian Hymns
Hymn 219 YESU Mbuyetu, mwafera
YESU Mbuyetu, mwafera
Mphulupulutu zanga,
Ndimo ndamva mund’itana,
Mutitu, Msachedwa.
Zonse za m’dziko zidzatha,
Koma za moyo m’Mwamba
Zomwe zidzakhalitsatu,
Chakatu ndi chaka.
Nyengo ifika, chenjera!
Adzakukana m’Mwamba.
Lapa zoipa zakozo,
Kuti ukaloŵe.