Chichewa Christian Hymns
Hymn 11 NDI mitima yokondwera,
NDI mitima yokondwera,
Mbuye wathu tiyamika.
E, chifundo chake chonse,
Ndi chosatha nthaŵi zonse.
Dzina lake tibukitsa,
Mlungu ndiye yekhayekha.
Mphamvu yake inalenga,
Dziko lonse ndi kumwamba.
Anatsogolera kale,
M’chipululu anthu ake.
Ndi chifundo atipenya,
Ife anthu osawuka.
Amaŵeta nyama zonse,
Zingasoŵe kanthu konse.
Tiimbire Mlungu wathu,
Waulemu ndi wamkulu.
Tithaŵire kwa Mulungu,
Ndiko tikapeze moyo.