Chichewa Christian Hymns
Hymn 106 MZIMU Woyera, mudzetu,
MZIMU Woyera, mudzetu,
Tiyeretsedwe m’mtimamu;
Mupatse anthu anuwa
Mitulo yanu yonseyo.
Kudzoza kwa Kumwambako
Kutitonthoza m’mtimamo,
Ndi kutidzutsa m’moyomu,
Tikhale okondanatu.
Pankhope pathu mthirepo
Chisomo chanu chijacho;
Mtendere mutininkhebe,
Mutiyendetse ponse phee!
Tionetseni tonsetu
Umodzi wanu wonsemo,
Atate, Mwana, Mzimu ’Nu
Tiimbe Nthaŵi zonsezo:
Titamire Nthaŵi zonse
’Tate, Mwana, Mzimu, Nonse.
Amen