Chichewa Christian Hymns
Hymn 275 NTHAWI yathu yafikatu,
NTHAWI yathu yafikatu,
Yoti tikagwire ntchito;
Monga Yesu ananena,
Panyanja ya Galileya.
Tikankhiretu kwakuya,
Ngakhale kuli zoopsa;
Ngakhale mafunde ali olimba,
Tidzapitabe mtsogolo.
Yesu anawauzatu,
Panyanja ya Galileya;
“Lero ndikusandutsani,
Kuti mudzasodze anthu.”
Ngakhale kuli mavuto,
Yesu ali kuyitana;
Mwa Iye tidzalimbika,
Ndipo tidzakhala naye.