Chichewa Christian Hymns
Hymn 5 ATATE wa Kumwambako,
ATATE wa Kumwambako,
Munawombola ife, ndi
Chikondi chanu chijacho;
Tiyamikira Inutu.
Ambuye Yesu Inutu,
Munabadwira anthu ’fe;
Munatifera tonse ’fe;
Tiyamikira Inutu.
Mzimu Woyera m’mtimamo
Tiyeretsedwe ndi Inutu;
Munatisunga bwinoli,
Tiyamikira Inutu.
Atate, Mwana, Mzimunso,
Ndinu Atatu, Mmodzitu
Ochimwa tikupemphani:
Mutikhululukire’fe