Chichewa Christian Hymns
Hymn 413 ZIPATA zachitsulo zitseguke zonse mbee!
ZIPATA zachitsulo zitseguke zonse mbee!
Ambuye wa Kumwambako aloŵe momwemo.
Mbendera yake ikupiza m’mlengalengamo,
Kufana ndi nyenyezi younika m’mdimamo.
Ankondo a Mulungu ’nu,
Yendani m’njiramo,
Mitima yanu yonseyo iyeretsedwe mbuu!
Tsatani Mbuye Yesuyo ndi mtanda wakewo;
Mlaliketu Uthenga kwa anthu onsewo.
Musamaopa kanthu ’yi tamani Yesuyo;
Kaimbireni nyimboyi ndi mphamvu zonse.
Zipata zatsegudwa mbee! za m’dziko monsemo;
Ambuye wapambanatu ndi mtanda wakewo.