Chichewa Christian Hymns
Hymn 404 YANG’ANA mtanda wa Yesu,
YANG’ANA mtanda wa Yesu,
Upeze moyo;
Chuma cha dziko chidzatha,
Yang’ana kwa Yesu.
Poyang’ana kwa Yesu Mbuye,
Pakuwona pamtanda wake,
Moyo ulipo.
Yesu alira pamtanda,
Kulilira ‘fe;
Kuti tilape zoipa,
Zomwe tichitazi.
Ambuye anatifera,
Pamtanda paja;
Kuti tikapeze moyo,
Kumwamba kwa Yesu.