Chichewa Christian Hymns
Hymn 23 TIIMBE nyimbo zotamanda
TIIMBE nyimbo zotamanda
Mulungu wathu wabwino,
Pakuti akondana nawo
Anthu okhala padziko;
Tero natuma Mwana wake,
Wakukondedwa kalelo,
Kutiphunzitsa ife tonse
Za chikondano chakecho.
Mulungu ndiye wachifundo,
Nadzalandira onsewa
Akuulula mphulupulu
Ndi kukondana ndi Yesu
Tilondelonde njira yake
Yopapatiza yaing’ono;
Adzatilondolera ndiye
Kutifikitsa m’Mwambamo.
Pakuwoloka mtsinje wa imfa
Dzanja Mbuyathu agwira;
Tikadagwira ntchito zake
Atipatsatu korona;
Komwe kulibe masauko,
Pena misozi maliro;
Mulungu tidzamtamandira,
Inde kosalekezanso.