Chichewa Christian Hymns
Hymn 212 NDI MISOZI, ndi chisoni,
NDI MISOZI, ndi chisoni,
Ndiliratu kwa Inu Yesu;
Ndi chifundo chandigwira,
Ndilira kutí ndili wanu
E! Kwa Inu, E! Kwa Inu!
Ndilira kuti ndili wanu.
Mbuye Yesu ndi Atate,
Mundiwona ndili wosowa;
Ndimasowa Mzimu wanu,
Kuinga zonse za mumtima.
Mtenderewo, wosanyenga,
Ndilira ine m’mtima mwanga;
Kundimvetsa chimwemwetu,
Ndilira ine m’mtima mwanga.
Kalekale ndinathawa,
Ndinakana kumvera Inu;
Koma lero ndamva kuti,
Muli mwini wake wa moyo.