Chichewa Christian Hymns
Hymn 147 MUSAŴALOLE mawuwo
MUSAŴALOLE mawuwo
Apite ngati mphepozi,
Musaumitse mtimatu,
Polira Yesu Mbuyedi.
Idzanitu, idzanitu,
Idzani kwa Ambuyeyo.
Idzanitu, idzanitu
Apulumutse inunso.
Musachitenso nthantha ’yi,
Mufulumire inutu;
Tsiku labwino nleroli,
Mulandirenso moyowu.
Zokondweretsa m’dzikomu
Nzosakhutitsa m’mtimamu,
Koma za Yesu zonsezo
Zikwaniritsa inudi.
Sakukanani Yesudi,
E, mukalapa m’mtimamo;
Lolani kuti Mzimuyo
Agwire ntchito zakezo.