Chichewa Christian Hymns
Hymn 128 ANTHU m’maiko onse
ANTHU m’maiko onse
Akhala mitundu;
Kapena m’dziko lino
Akhala anzathu;
Agona mwa zoipa,
Apulukiradi,
Ati, Mutilangize
Abale, bwerani.
Ngakhale alemera
Ndi chuma cha dziko,
Kodi akakondwera
Opanda Mulungu?
Kodi akhala mwaŵi
Otsata zawozo?
Iyai, awonongeka,
Apeza tsokalo.
Ndi ife akudziŵa
Chikondi cha Mlungu,
Kodi tidzaŵamana
Kuŵala kwa Kristu?
Chipulumutso! Inde,
Tichibukitsetu,
Kuti mitundu yonse
Ibwere kwa Yesu.
Akristu nyamulani
Maneno a Mulunguyo,
Ndi moyo lalikani
Pa dziko lonselo;
Ndi Yesu Mpulumutsi
Anatiferatu;
Adzabvomera onse;
Ndi Mwana wa Mlungu.