Chichewa Christian Hymns
Hymn 436 YEHOVA Mlungu wathu,
YEHOVA Mlungu wathu,
Amene mumapatsa
Zipatso za chikondi
Polenga anthu anu,
Mupatse awa ‘ŵiri
Mitima yokondwetsa,
Yofana m’munda muja
Munayendamo kale.
Mbuyathu wokondedwa,
Pokhala m’dziko muno
Munadza ku ukwati,
Naŵadalitsa onse;
Ukwatiwu mukonze,
Mukhale nafe pano;
Iwowa m’ŵadalitse
M’chifundo chanu chonse.
Ndi Mzimutu Woyera
Mufike nayo mphamvu,
Mukatsangane nawo
Akupangana omwe;
Mupatse ’wo chisomo
Chokometsetsa mtima;
Chikuletu chikondi
Chitsazo nchanu chomwe.
Mulungu mwa Atatu,
Atate, Mwana, Mzimu,
Tikhaletu wokondwa
Ndi Inu m’chiyanjano;
Titama Inu Mlungu,
Wokonda ife ndinu;
M’ulendo wathu wonse
Tiyende m’chikondano.