Chichewa Christian Hymns
Hymn 305 NDALIMVA dziko la m’talimo,
NDALIMVA dziko la m’talimo,
Munthu sangathe kulisimba;
Malowo awala koposa,
Ndi Yesu tidzakhala naye.
Komweko, komweko,
Ndi Yesu tidzakhala naye.
Musazengereze anthuni,
Chimwemwe uko chilipodi;
Anthuni, mudzalandiradi,
Ndi Yesu mudzakhala naye.
Mwana’we pereka mtima’ko,
Akuchotsere zoipazo;
Udzakhala wokondweradi,
E! n’kwabwino lola mwana ‘we.
Idzani, mverani, lapani,
Chipulumutso chilipodi;
Kwa Yesu yemwe wofera ‘nu,
Ndi Yesu mudzanka
Kumwamba.