Chichewa Christian Hymns
Hymn 266 MBUYE ndamva mwawazira
MBUYE ndamva mwawazira
Anthu ena madalitso;
Mvula yanu yawagwera;
Mbuye, ine mudalitse.
Etu ine, etu ine,
Mbuye, ine mudalitse.
’Tate, msandipitirire,
Ndimaipa mtima ine;
Ndiyenera munditaye,
Koma mukhululukire.
Yesu, msandipitirire
Kuti ndinu ndikondane;
Ndinalira Inu Mbuye,
Msandileke poitana.
Mzimu, msandipitirire,
Mupenyetsatu akhungu
Mboniyo ya Mbuye Yesu,
Mundipatse ine mphamvu.
Ndinagona mwa zoipa,
Ndinakunyozani ine,
Dziko lino ndinakonda,
Mbuye, mukhululukire.
Ha! chikondi cha Mulungu,
Mwazi wa Mbuyathu Yesu,
Chiyanjano cha Mzimuyo
Zonse zidzalemekeza.