Chichewa Christian Hymns
Hymn 113 KALERO anthu onse
KALERO anthu onse
Nachimwa kwa Mulungu
Mulungu anawona
Nawona tchimo lawo,
Nafuna kwawononga,
Nafuna kwawononga.
Mulungu anatuma,
Natuma mvula ija,
Nadzaza dziko lonse
Anafa anthu onse,
Anafa m’mvula muja,
Anafa m’mvula muja.
Mulungu anatuma,
Natuma Nowa uja,
Wamanga chombo chake,
Ndi chachitalitali,
Nowayo nayendamo,
Nowayo nayendamo.
Nowayo anatuma,
Natuma chikwangwala,
Chatsika pansi pansi,
Chosabwerera konse,
Chithaŵa m’talitali,
Chithaŵa m’talitali.
Kutuma wabwereza,
Natuma nkhunda ija,
Yatsika pamadzipo,
Yathyolatu mayani,
Yampatsa Nowa yemwe,
Yampatsa Nowa yemwe.
Kalelo Mbuye Yesu
’Nafera anthu onse,
Ndiyeyo chombo chathu,
Tikabisala mommo
Tipulumuka mommo,
Tipulumuka mommo.