Chichewa Christian Hymns
Hymn 104 MUBWERE Mzimu Inu
MUBWERE Mzimu Inu
Woyera, wakufatsa,
Muchotse mdima m’mtima mwathu
Tikapenye m’maso.
Mtisangalatse m’zonse,
Ndi wachifundo Inu,
Tiyembekeze kumapazi
A Mbuyathu Yesu.
Mtitsitsimutse ife
Kuchotsa nkhaŵa zathu,
Muyatse moto wachikondi
Mu mitima yathu.
Mtitsutse titachimwa
kutilapitsa m’mtima,
Mwonetsenso chikondi chokhululukira tchimo.
Kutiyeretsa m’mtima
Ndi ntchito yanu yokha,
Kupatsa moyo watsopano
M’mene timafoka.
Mukhale m’kati mwathu,
Mutichotsere mantha,
Tidzayamika ’Tate wathu,
Mwana wawo ndi ’Nu.