Chichewa Christian Hymns
Hymn 194 AMBUYE’naitan’ne;
AMBUYE’naitan’ne;
“Dzapumulire kuno,
Tsamira mutu, mwana’we
M’chifuwa mwanga muno.”
Ndabwera kwa Ambuyeyo;
Wolema, wachisoni;
Anandipulumutsako,
Nakondweretsa ine.
Ambuye naitana’ne;
“Ndipatsa anthu madzi,
Wotopa ndi waludzu’we
Dzamwere moyo kuno.”
Ndabwera kwa Ambuyeyo.
Ndamwera madzi awa;
Laleka ndithu ludzulo,
Tsopano moyo wadza
Ambuye naitana’ne;
“La dziko ndine Dzuŵa,
Yang’ana Ine, kwacha’we,
Wachoka mdima uja.”
Ndayang’anira Mbuyeyo
Ndzapeza Dzuŵa langa
Londiyendetsa bwinoli
Pa njira yanga yonse.