Chichewa Christian Hymns
Hymn 337 PADZIKO pano tikhalira M’moyo wosauka;
PADZIKO pano tikhalira M’moyo wosauka;
Komatu kwa Mulungu kuli
Dziko lakudala;
Mbuyathu Yesu wapitako,
Iye ’natsogola;
Tidzamtsatira ife tonse,
Tsiku lomaliza.
Tiyeni, tiyeni,
Ku dziko lakudala;
Tidzafikira m’dziko ilo
Tsiku lomaliza.
Masiku tikatsala ife
M’dziko mwathu momwe
Mulungu watipatsa ntchito,
Tikazigwiritse.
Pamene zakuipa zathu
Zisautsa ife,
Tikapemphere Mbuye wathu,
Atipulumutse.
Ulendo wathu ukadzatha
Tidzafika kwathu,
Adzatifitsa ife komwe
Yesu Mbuye wathu.
Sitidzapeza masautso
M’dziko la Mulungu,
Tidzakondwera chikondwere
Nthaŵi zathu zonse.