Chichewa Christian Hymns
Hymn 111 YAKOBO mwanatu wachinyengoyo;
YAKOBO mwanatu wachinyengoyo;
Wanyenga bambo ake
Kuti, “Inetu ndinetu
Esau mwana wanu.”
Esau analira, “abambo
Inu, abambo anga,
Ndabwera nayo nyama,
Mulandire, mudye.”
Thupi ndi Esau, koma mawuwo,
Ngatitu a Yakobo;
“Bwera mwana wanga,
Bwera pafupi n’kusisite.”
Ndapezatu bwenzi latsopanolo,
Ndi Yesu Mpulumutsi;
Yemwe angathe, kuchotsa,
Machimo anga onse.
Machimo andizunza ine;
Mtima mwangamu inedi,
Ndifuna Inu Mbuye,
Mulowe m’mtima mwanga.