Chichewa Christian Hymns
Hymn 101 MZIMU Woyera, mudze mumitima mwathumo,
MZIMU Woyera, mudze mumitima mwathumo,
Mufike nazo mphamvu zanu zazikuluzo.
Mufike monga nyali younika m’mtimamo.
Mutidziŵitse zakuipa zakukhalamo.
Mufike monga moto wakuotcha zomwezo.
Mutiyeretse ifetu m’mitima mwathumo.
Mufike monga ngati njiŵa yamtenderewo.
Kutitu anthu anu onse akondanetu.
Mufike monga ngati mphepo yokokomayo,
Tikhale tonse nazo mphamvu zanu zonsezo.