Chichewa Christian Hymns
Hymn 69 KONDWERANI dzuŵa lino,
KONDWERANI dzuŵa lino,
Aleluya.
Yesu wanka m’Mwamba momwe:
Aleluya.
Wachokera m’dziko lino,
Aleluya.
Wabwerera kwawo komwe.
Aleluya.
Zomkwezetsa zili m’Mwamba,
Aleluya.
Zodikira Mbuye wathu;
Aleluya.
Mloŵetseni n’kumlambira,
Aleluya.
Mfumu yathu yaulemu.
Aleluya.
Yesu nkana saoneka,
Aleluya
Atipempherera komwe:
Aleluya.
M’nyumba yake yokonzeka
Aleluya.
Atilinda ife tomwe
Aleluya.
Tiyamike Dzina lake,
Aleluya.
Mfumu ya ulemu wonse.
Aleluya.
Tibukitse mbiri yake
Aleluya.
Pansipa padziko lonse.
Aleluya.