Chichewa Christian Hymns
Hymn 478 YESU atiuza tiŵale ’fe.
YESU atiuza tiŵale ’fe.
Monga nyali m’mdima tiunike mbee!
Pansi pali mdima ŵalanitu,
Inu m’malo mwanu ndi ine ’mu.
Yesu atiuza tiyambemo,
Ationa bwino ndi kuŵalako;
Ayang’ana pansi poŵala ’fe,
Inu m’malo mwanu ndi ine ’mu.
Yesu atiuza tiŵale pa
Anthu ali m’mdima osaukawa;
Tiŵalire onse, tonsefetu,
Inu m’malo mwanu ndi ine ’mu.