Chichewa Christian Hymns
Hymn 228 MWAKHULUPIRIRADI
MWAKHULUPIRIRADI
Yesu Ambuyathu;
Muli nazo zakezo,
Zidzatu zinanso.
Mlungu wachisomocho
Mbuye wathu ndiye,
Ati zinthu zonsezo
Nzathu mwa Iyeyo.
(Zina ndi zinanzo
Zidza kwa ifedi,
Inde mtima wakewo
Uli wokomadi.)
Mwamva Yesu m’mtimamo,
Adzanso kaŵiri,
M’mene ali nanutu
Muli ndi Chimwemwe.
Ntchito zachifundozi
Iye watha izi,
Kuti mwawo m’Mwambamo
Naye tikhalebe.
Mwamva Mzimu wakewo,
Zake zimvekanso
Kugwa ngati mvulayo
Yachisomo chake.
Mzimu ndiye mphamvudi
M’moyo mwathu muno,
Mpaka tidzafikako
Komwe kuli Yesu