Chichewa Christian Hymns
Hymn 22 MU ZONSE abale yamikani,
MU ZONSE abale yamikani,
Mulungu ndi wamkulu,
Adziwa kupatsa anthu ake,
Zomwe iwo akuzisowa.
Akhrisitu pamavuto tiyeni timulemekeze,
Pamtendere tiyeni timulemekeze.
Maso ake ali pa anthu,
Okhala m’dziko lapansi.
Mu zonse abale yamikani,
Mulungu ndi wamkulu,
Adziwa kuveka anthu ake,
Ngakhale nyama zakuthengo.
Mu zonse abale yamikani,
Mulungu ndi wamkulu,
Adziwa kupatsa mphatso zake,
Ngakhalenso kwa tiŵanato.