Chichewa Christian Hymns
Hymn 21 KUZANI Mlungu m’Mwambamo,
KUZANI Mlungu m’Mwambamo,
Mtamande m’kuyanso;
Nzozizwa nkhani zakezo,
Njolimba ntchito njo!
Pochimwa anthu onsewo
Nja Mlungu nzeruyi;
Adamu wachiŵiriyo
Wathetsa tchimoli.
Thupi la mwazi wathu ’li
Lochimwa kalelo,
Labweranso ku nkhondoyi,
Laposa monsemo.
Choposa nalo thupilo
Chikhale momwemu,
Chiyeretsetsa m’katimo,
Ndi Mulungu Iyeyu.
Anatikondakonda ’Ye,
Ndi Mlungu Iyeyo,
Anatifera anthu ’fe
Ndi Mulungu Iyenso.
Ndi m’munda muja chete, phee!
Pamtanda pati njo!
Anaphunzitsa’bale ’fe
Titero ifenso.
Kuuzani Mlungu m’Mwambamo
Mtamande m’kuyanso;
Nzozizwa nkhani zakezo,
Njolimba ntchito njo!