Chichewa Christian Hymns
Hymn 16 MTIMA wanga lemekeza,
MTIMA wanga lemekeza,
Mlungu wako ndi chimwemwe;
Nthaŵi zonse ndi m’tamanda,
Ndimwimbira nyimbo zanga.
Moyo, mphamvu, nzeru zonse,
Zidzam’lekeza konse.
Ndi wamwayi munthu uja,
Am’thandiza Mbuye wake;
Akachita mantha iye,
Am’chotsera nkhaŵa yake;
Ndipo likam’gwera tsoka,
Amakhulupi’ra kokha.
Mbuye ndiye wachifundo,
Achiritsa akudwala;
Anyamula akufoka,
Naŵadyetsatu anjala.
Wakusunga mlendo ndiye,
Nathandiza amasiye.
Ndiye Mbuye wa ambuye,
Mphamvu yake ndi yokwana;
Adzakhala chikhalire.
Mfumu yathu yopambana.
Aleluya! Kondwerani!
Mlungu wathu yamikani.