Chichewa Christian Hymns
Hymn 135 USANABADWE, Yeremiya,
USANABADWE, Yeremiya,
Ine ndinakudziwa;
Ndipo ndinakupatula,
Kuti ukhale mneneri.
Ulalike mawu anga Yeremiya,
Pita ukalalikire
Mawu anga;
Mawu anga Yeremiya.
“Usaopetu nkhope zawo,
Ine ndili ndi iwe;
Kuti ndikulanditsetu,
Iweyo,” ati Yehova.
Usaganize ndiwe mwana,
Iwe udzanka konse;
Kumene ndidzakutuma,
Kuti ukalalikire.