Chichewa Christian Hymns
Hymn 112 ELISA mneneri,
ELISA mneneri,
Wachita zamphamvu;
Kuyandamitsa nkhwangwayo,
Pa Yolodani’po.
(M) Nkhwangwayo,
(O) Ndiyobwereka,
Nalira mnyamatayo;
Popeza ndiyobwereka,
Pa Yolodanipo.
Elisa mneneri,
Natenga kamtengo;
Naponya pamadzi paja,
Nkhwangwa niyandama.
Mulungu wamphamvu,
Natuma Mwana ‘ke;
Kuti atifere ife,
Kutipulumutsa.
Nanga ife lero,
Kodi takonzeka;
Kusiya machimo athu,
Kutsata Yesuyo?