Chichewa Christian Hymns
Hymn 214 KUNALI munthu ku Yeriko,
KUNALI munthu ku Yeriko,
Dzina lake Zakeyu;
Anali munthu wamkulu,
Wokhometsa misonkho.
(M) Kunali Zakeyu,
(O) Ku Yeriko,
(M) Nafunafuna,
(O) Kuwona Yesu,
(M) Koma chifukwa,
(O) Cha khamulo,
Anakwera mumtengo.
Paulendowo Ambuyeyo,
Anafika pamtengo;
Nayang’ana m’mwamba muja,
Anawona Zakeyu,
Ambuye Yesu nanenadi,
“Fulumira nutsike;
Lero lino ndiyenera,
Kukhala m’nyumba mwako.”
Zakoyuyo mofulumira,
Anatsika mumtengo,
Anam’tenga Mbuye Yesu,
Kuti akam’chereze,
Anadandauladi ena,
“Ambuye wachitanji?
Bwanji Iye analowa,
M’nyumba ya wochimwayo?”
Zakeyuyo pakumva ichi,
Anawuza Ambuye:
“Theka la chuma changacho,
Ndidzapatsa osowa.”
Leronso chipulumutsochi,
Chagwera m’nyumba yathu;
Tilape zoipa zathu,
Kutí tipulumuke.