Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 78 ALINKUDZA wansoni Munthu,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 78 ALINKUDZA wansoni Munthu,

 

ALINKUDZA wansoni Munthu,
Wakukhala Kumwamba;
Alinkudza m’ulemerero,
Ndi Mwamuna wa mtanda.

Aleluya, Aleluya,
Alinkudza kwa ife;
Ndi chimwemwe
Tidzamkomana,
Pakufika Ambuye.

Alinkudza Ambuye Yesu,
Wakuphedwa pa dziko;
Alinkudza kukhala Mfumu,
Yoweruza mayiko.

Pakufika asonkhanitsa,
Anthu ake oyera;
Adzafuna mitundu yonse,
Omwe Iye ‘nafera.

Exit mobile version