Chichewa Christian Hymns
Hymn 77 MMENE Yesu adzabwera,
MMENE Yesu adzabwera,
Adza ndi mitambo;
Ndipo diso lililonse,
Lidzamuwona Iye.
Adza, adza,
Adza ndi mitambo,
Ndipo diso lililonse;
Lidzamuwona Iye.
Adzakhala pa chimpando,
Choweruziracho;
Nadzayamba kuweruza,
Milandu ya anthu’fe.
Angelo ‘dzagwira ntchito,
Yolekanitsadi;
Anthu onse a padziko,
M’magulu awiritu.
Olugama nadzayima,
Kudzanja lamanja;
Koma onse oyipawo,
Mbali yakumanzere.
Akudzanja lamanjalo,
Kumoyo wosatha;
Akudzanja lamanzere,
Kumoto Wosathawo.
