Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 67 PAMENEPO pokhala madzulo,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 67 PAMENEPO pokhala madzulo,

 

PAMENEPO pokhala madzulo,
Tsiku loyamba la Sabata;
Chifukwa chakuopa a Yuda,
Makomo ali chitsekere.

Yesu anadza naimilira,
Pakati pa ophunzirawo,
Yesu nanena mawuwo nati:
“Mtendere ukhale ndi inu.

Pameneponso Yesu Ambuye,
Naonetsatu Tomasiyo;
Manja akewo ndi nthiti zake,
Tomasi nati: “Mlungu wanga.

Odala iwo okhulupira,
Ngakhale iwo sanaone;
Chifukwa iwo adzalandira,
Moyo wosatha kwa Atate.

Exit mobile version