Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 49 ONA Mwanawankhosayo

Chichewa Christian Hymns

Hymn 49 ONA Mwanawankhosayo

 

ONA Mwanawankhosayo
Wakuseza zakuipa zathu zonse.

Mwana wankhosa
Watisenzera
Zakuipa zathu zonse.

Anazenza m’thupi mwake;
Pakukhomedwa pa mtanda anali duu.

Ona pamtanda Yesuyo
Anabvutika chifukwa cha anthu’fe.

Imva kulira kwa Yesu
Pamene anasiyidwa muimfayo.

M’mwazi wake tisambamo;
Zichotsedwa zakuipa zathu zonse.

(Ona Mwana wa nkhosayo
Wakusenza zakuipa, zathu zonse.)

Exit mobile version