Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 483 NTHAŴI yaubwana yatha,

Chichewa Christian Hymns

Hymn 483 NTHAŴI yaubwana yatha,

 

NTHAŴI yaubwana yatha,
Sukulu yathu yathanso;
Nkhaŵa ndizoŵaŵa zomwe
Zitibisaliranso.

Yesu wakufatsa mtima
Mlendo pansi pano ’Ye,
’Natifera, natisunga,
Atitsogolere ’fe.

Tamverani, aitana;
“Ana, munditsatetu,”
Yesu, tisapite kwina,
Tizikutsatani ’Nu.

Posachedwa tilekana
Osalankhulananso,
Koma tidzaona tonse
Wina mnzake m’Mwambamo.

Exit mobile version