Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 469 NDIKONDA mbiri yomwe

Chichewa Christian Hymns

Hymn 469 NDIKONDA mbiri yomwe

 

NDIKONDA mbiri yomwe
Ya amithengawo
Ya Mbuye, Mfumu yathu
Pofika pansipa;
Zochimwa zindizinga,
Koma ndidziŵatu
Anawombola ine
Pakundikondadi.

Ndikondwa kuti Yesu ’Nakhala mwanatu,
Chitsanzo atipatsa
Cha moyo wakewo;
Ndikati ndimtsatire
Zochita zakezo,
Sadzandinyoza konse
Pakundikondadi.

Pakumyamika Iye
Ndidzamwimbiratu;
Ngakhale sindimwona
Amandimveradi;
Pakuti walonjeza
Adzalandira ’ne
Ndiimbe ndi angelo,
Pakundikondadi.

Exit mobile version