Site icon Treasure Hymns – Chichewa

Hymn 450 YESU, munditsogoza

Chichewa Christian Hymns

Hymn 450 YESU, munditsogoza

 

YESU, munditsogoza
M’njira yanga yonseyo;
Wakunditsogozatu
Ndinu, mundisungetu;
Inde, paulendowo
Mundisunge kolimba.

Monga may’asusunza
Mwana wake polira,
Wakunditonthozatu
Ndinu, munditonthoze,
Ine, m’njira yanuyi
Munditsogoleretu.

Mbuye, ndinu wamphamvu,
Mumatola ananu.
Anthu onse pansipa
Ali otaikatu;
Muchitire chifundo,
Muŵatole onsewo.

Exit mobile version